A Malawi awalangiza kuti ayike chidwi chawo pa nkhani ya ulimi othilira pogwirita ntchito zipangizo za luso loyendela mphepo. Mkulu wa Kampani ya Africa Windmill a Gibozi Mphanzi ndi amene anena izi m’mzinda wa Lilongwe. A Mphanzi ati anthu amene anawaikila zinthu anga izi akhala akupeza phindu kuchokera mu ulimi odalira zipangizo zoyendera mphepo. A Mphanzi ati alimi ambiri apeza ndalama monga ma K1 Million wena ma K800,000. Pakadali pano a Mphanzi apempha a Malawi kuti ayambe kugwiritsa ntchito zipangizo izi chifukwa sizikhala ndi zambiri zolowetsa. Kampani ya Windmill Africa ipempha a Malawi kuti ayambe kugwiritsa ntchito zipangizo zoyendera mphepo Post navigation Wateraid allocates 2.537 Billion kwacha to address water issues in Ntchisi Prophet Nyasulu brings portable water to Dowa hard to reach area