Bungwe la United Nations (UN) layamikila mtsogogoleri wadziko lino a Dr Lazarus McCarthy Chakwera kamba koonetsa chidwi pa ntchito yotukula amai mdziko muno. Rebecca Adda-Dontoh walankhula izi dzulo pame mtsogoleri wadziko lino anakumana anthu ogwira ntchito kumabungwe a UN. M’mawu awo a Dontoh anayamikila a Chakwera kuti amai akusimba lokoma mdziko muno chifukwa chakwera akuwapatsa mpata otsogolera nawo mzochitika chitika za dziko. A Dontoh anayamikilaso a Chakwera kamba ka ma ufulu wachibadidwe omwe a Malawi akusangalala nawo. “Ngakhale UN ndi yokondwa komanso maiko ambiri akukondwa ndimmene nkhani za ma ufulu zikuyendera mdziko muno,” adatero a Dontoh. Mmawu ake Mtsogoleri adziko lino adayamikila ma bungwe a UN kamba ka thandizo lomwe akupereka kudziko lino la Malawi. Iwo anapereka chitsanzo cha mmene UN idathamangira pa nthawi ya ngozi ya Namondwe omwe anachitika chaka chatha. Post navigation President Chakwera receives rare praise from Parliamentarians – the case of Zomba Malosa MP Kezzie Msukwa thankful to the president for changing the face of Chitipa East