Mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus McCarthy Chakwera apempha a Malawi mdziko muno kuti apewe mkhalidwe odzikonda podziunjikila ndalama kudzera mnjira yakuba ndi katangale.

A Chakwera amayankhula izi pamsomkhano wa chitukuko omwe anachititsa pa sukulu ya Katerele uku ndi Salima.

A Chakwera analimbikitsa ogwira ntchito mboma kuti akuyenera kugwiritsa ntchito bwino ndalama zaboma zomwe ndi za a Malawi.

DR LAZARUS CHAKWERA

Pamsonkhano umenewo a Chakwera analandila a Uladi Mussa omwe alowa mchipani cha Malawi Congress (MCP).

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *