Mtsongoleri wa dziko lino a Dr Lazarus McCarthy Chakwera wati ndi okhudzidwa ndinso a Chisoni ndi imfa ya yemwe adali mtsogoleri wa dziko la Namibia a Dr Gage Gottfried Geingob. A Geingob adamwalira pa 4 February, 2024 patangotha mwezi umodzi atalengeza kuti iwo apezeka ndi matenda a Khansa. Chakwera kupereka ulemu otsiliza A Chakwera ali mu dziko la Namibia pomwe iwo ndi nthumwi zina zili mdzikolo kukhuza maliro a olemekezeka a Geingob. A Chakwera ati imfa ya Geingob yankhuza Africa komanso dziko lonse lapansi kamba kakuti a Geingob adali munthu olimbikira pa nkhani zolimbikitsa mtendere. Post navigation Governance expert Undule Mwakasungula weighs in on budget Prophet Nyasulu, Kingdom Care International donates houses to needy families in Dowa