Mkhalakale pa ndale a Ken Msonda adzudzula chipani cha Democratic Progressive (DPP) kamba ka mkhalidwe wake oloza zala kwa anthu wena pamene mavuto akuchoka kwawo komweko.

Ken Msonda : DPP ikulakwitsa

Mukulankhula kwawo a Msonda apereka chitsanzo cha ziwawa zomwe zidachitika pa Mbowe.

Iwo ati palibe amene angapite kukamenya otsatira a chipani cha DPP pakadali pano kupatula okha okha.

“Ku DPP kuli magulu magulu omwe akulimbirana ma udindo. Nkhondo ikuchokera komweko, ” adatero a Msonda.

Iwo adati mbiri yaziwawa yagona ku DPP. “Kodi adapha Chasowa ndi ndani, nanga Issa Njaunju adapha ndindani?”adafunsa a Msonda.

A Msonda adapitiliza kufunsa kuti kodi amene amaotcha misika ndinso kuotcha ma nyumba awanthu ndindani , ndimayesa ndi DPP.

“DPP ndi chipani chomwe chikulephera kukonza zinthu zake akatero amafuna kupaka anthu wena,” adatero a Msonda.

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *