Mtsogoleri wadziko lino a Dr Lazarus Chakwera wati ndi odandaula ndi imfa ya yemwe adali nduna yakale yaboma yoona za malamulo a Raphael Kasambara. A Kasambara adamwalira dzana pa 7 June , 2024, mchipinda momwe iwo amagona ku Damron Lodge ku Lilongwe. Koma mukulankhula kwawo, a Chakwera adati, iwo pamodzi ndi mai wafuko a Monica Chakwera ndi okhudzidwa kwambiti kamba koti a Kasambara adali munthu olimbikira kwambiri kutumikira dziko lino pankhani za Malamulo. A Chakwera ati, a Kasambara adali munthu odzipereka kwambiri panthawi yomwe iwo amagwira ntchito ku boma ngati nduna yoona nkhani za Malamulo. Mwa ichi a Chakwera ati a Malawi adzawasowa a Kasambara maka luso lawo pa ukadaulo wa malamulo. Post navigation President Chakwera mourns Ex- Minister of Justice Raphael Kasambara ABIDA MIA ALONJEDZA KUPITILIZA KUTUKULA CHIKWAWA NKOMBEDZI